Hadith Collection - Into Chichewa

Hadith Collection - Into Chichewa

Share

Cholinga changa ndikufalitsa uthenga wa Mulungu muchilankhulo chimene timamva. Pempho langa ndi loti pangani follow kuti hadith iliyonse isamakuphonyeni.

Ndine (translator) M'bale wanu Abuwbakr Size, Zikomo

17/11/2025

'Umar (Mulungu asangalale naye) adati: Mtumiki ﷺ adanena kuti,

"Usiku wathawu wina wake, wochokera kwa Ambuye wanga, anadza kwaine (mkulota) pomwe ndinali mu (chigwa cha) 'Aqiq nati kwa ine, "Pemphera (swalah) mu chigwa ichi chodalitsika ndipo unene: "Labbaik" pa 'Umra ndi Hajj."

أَنَّ عُمَرَ ـ رضى الله عنه ـ حَدَّثَهُ قَالَ حَدَّثَنِي النَّبِيُّ صلى الله عليه وسلم قَالَ ‏"‏ أَتَانِي اللَّيْلَةَ آتٍ مِنْ رَبِّي وَهْوَ بِالْعَقِيقِ أَنْ صَلِّ فِي هَذَا الْوَادِي الْمُبَارَكِ وَقُلْ عُمْرَةٌ وَحَجَّةٌ ‏"‏‏ (وَقَالَ هَارُونُ بْنُ إِسْمَاعِيلَ حَدَّثَنَا عَلِيٌّ عُمْرَةٌ فِي حَجَّةٍ‏.‏ )


Sahih al-Bukhari, 7343
Vol. 9, Book 92, Hadith 442
Book of holding fast to the

17/11/2025

Abu Burda (Mulungu asangalale naye) adati,

"Pamene ndinafika ku Madina, 'Abdullah bin Salam anakumana nane ndipo anati kwa ine, "Nditsateni kunyumba yanga kuti ndikakupangileni chakumwa mu kapu imene Mtumiki ﷺ ankamwera, ndikutinso ukapemphere Swalah mu mzikiti umene Mtumiki ﷺ anali kupemphera."

Choncho ndinapita naye (limodzi), ndipo anandimwetsa Sawiq ndikundipatsa tende kuti ndidye. Ndipo kenako ndinadzapemphera mu mzikiti wake (umene Mtumiki ﷺ anapemphereramo).

عَنْ أَبِي بُرْدَةَ، قَالَ قَدِمْتُ الْمَدِينَةَ فَلَقِيَنِي عَبْدُ اللَّهِ بْنُ سَلاَمٍ فَقَالَ لِي انْطَلِقْ إِلَى الْمَنْزِلِ فَأَسْقِيَكَ فِي قَدَحٍ شَرِبَ فِيهِ رَسُولُ اللَّهِ صلى الله عليه وسلم، وَتُصَلِّي فِي مَسْجِدٍ صَلَّى فِيهِ النَّبِيُّ صلى الله عليه وسلم‏.‏ فَانْطَلَقْتُ مَعَهُ، فَسَقَانِي سَوِيقًا، وَأَطْعَمَنِي تَمْرًا، وَصَلَّيْتُ فِي مَسْجِدِهِ‏.‏"

Sahih al-Bukhari, 7342
Vol. 9, Book 92, Hadith 441
Book of holding fast to the


17/11/2025

Anas (Mulungu asangalale naye) adati,

"Mtumiki ﷺ anapangitsa chiyanjano pakati pa anthu a Ansar ndi MaQuraish mu nyumba yanga ya ku-Madina.

Ndiponso Mtumiki ﷺ adawapemphera anthu a Bani Sulaim (themberero) kwa Mwezi umodzi (mu raka'at yomaliza ya Swalah iliyonse ya Fardh)."

عَنْ أَنَسٍ، قَالَ حَالَفَ النَّبِيُّ صلى الله عليه وسلم بَيْنَ الأَنْصَارِ وَقُرَيْشٍ فِي دَارِي الَّتِي بِالْمَدِينَةِ‏.‏ وَقَنَتَ شَهْرًا يَدْعُو عَلَى أَحْيَاءٍ مِنْ بَنِي سُلَيْمٍ"

Sahih al-Bukhari, 7340, 7341
Vol. 9, Book 92, Hadith 440
Book of holding fast to the


17/11/2025

Aisha (Mulungu asangalale naye) adati,

"Ndowa iyi (yamadzi) inali kuikilidwira ine ndi Mtumiki ﷺ, ndipo (ife) tinkatunga (madzi) m'menemo limodzi (posamba)."

عَائِشَةَ، قَالَتْ كَانَ يُوضَعُ لِي وَلِرَسُولِ اللَّهِ صلى الله عليه وسلم هَذَا الْمِرْكَنُ فَنَشْرَعُ فِيهِ جَمِيعًا‏.‏"

Sahih al-Bukhari, 7339
Vol. 9, Book 92, Hadith 439
Book of holding fast to the


04/09/2025

As-Sa'id bin Yazid (Mulungu asangalale naye) adanena kuti iye

"Adamumva 'Uthman bin 'Affan akupanga Khutuba pa mimbali ya Mtumiki ﷺ.

"حَدَّثَنَا أَبُو الْيَمَانِ، أَخْبَرَنَا شُعَيْبٌ، عَنِ الزُّهْرِيِّ، أَخْبَرَنِي السَّائِبُ بْنُ يَزِيدَ، سَمِعَ عُثْمَانَ بْنَ عَفَّانَ، خَطَبَنَا عَلَى مِنْبَرِ النَّبِيِّ صلى الله عليه وسلم‏.‏"

Sahih al-Bukhari, 7338
Vol. 9, Book 92, Hadith 438
Book of holding fast to the


04/09/2025

Ibn 'Umar (رضى الله عنهما) adati,

"Ndidamumva 'Umar (bin Al-Khattab, akupanga Khutuba) pa Mimbali ya Mtumiki ﷺ

"حَدَّثَنَا قُتَيْبَةُ عَنْ لَيْثٍ عَنْ نَافِعٍ عَنِ ابْنِ عُمَرَ‏‏ ح. وَحَدَّثَنِي إِسْحَاقُ، أَخْبَرَنَا عِيسَى، وَابْنُ، إِدْرِيسَ وَابْنُ أَبِي غَنِيَّةَ عَنْ أَبِي حَيَّانَ، عَنِ الشَّعْبِيِّ، عَنِ ابْنِ عُمَرَ ـ رضى الله عنهما ـ قَالَ سَمِعْتُ عُمَرَ، عَلَى مِنْبَرِ النَّبِيِّ صلى الله عليه وسلم‏.‏"

Sahih al-Bukhari, 7337
Vol. 9, Book 92, Hadith 437
Book of holding fast to the


14/07/2025

Nafi' (Mulungu asangalale naye) adati: Abdullah adanena kuti,

"Mtumiki ﷺ adakonza mpikisano wothamangitsana pa bulu, ndipo bulu zokonzeredwa mpikisanowo zinkapatsidwa chakudya chochepa kwa masiku amenewo (mpikisanowo usanachilitike ndicholinga chakuti buluzo zipambane). Choncho mpikisanowo unali wothamanga kuchokera pa Al-Hafya kukafika ku Thaniyat-al-Wada. Ndipo bulu zosakonzekerezedwa zinali kuthamanga kuchokera pakati pa Thaniyat-al-Wada ndi mzikiti wa Bani Zuraiq,"

'Abdullah anali m'modzi wa iwo amene anatenga nawo gawo pa mpikisanowo.

"حَدَّثَنَا مُوسَى بْنُ إِسْمَاعِيلَ، حَدَّثَنَا جُوَيْرِيَةُ، عَنْ نَافِعٍ، عَنْ عَبْدِ اللَّهِ، قَالَ سَابَقَ النَّبِيُّ صلى الله عليه وسلم بَيْنَ الْخَيْلِ، فَأُرْسِلَتِ الَّتِي ضُمِّرَتْ مِنْهَا وَأَمَدُهَا إِلَى الْحَفْيَاءِ إِلَى ثَنِيَّةِ الْوَدَاعِ، وَالَّتِي لَمْ تُضَمَّرْ أَمَدُهَا ثَنِيَّةُ الْوَدَاعِ إِلَى مَسْجِدِ بَنِي زُرَيْقٍ، وَأَنَّ عَبْدَ اللَّهِ كَانَ فِيمَنْ سَابَقَ‏.‏ حَدَّثَنَا قُتَيْبَةُ عَنْ لَيْثٍ عَنْ نَافِعٍ عَنِ ابْنِ عُمَرَ‏.‏"

Sahih al-Bukhari, 7336
Vol. 9, Book 92, Hadith 436
Book of holding fast to the


14/07/2025

Abu Huraira (Mulungu asangalale naye) adati: Mtumiki ﷺ adanena kuti,

"Pakati pa mnyumba yanga ndi mimbali yanga pali munda wochokera mu minda yaku Jannah, ndipo mimbali yanga ili pamwamba pa thanki ya mntsinje wanga (wotchedwa Al-Kauthar)."

حَدَّثَنَا عَمْرُو بْنُ عَلِيٍّ، حَدَّثَنَا عَبْدُ الرَّحْمَنِ بْنُ مَهْدِيٍّ، حَدَّثَنَا مَالِكٌ، عَنْ خُبَيْبِ بْنِ عَبْدِ الرَّحْمَنِ، عَنْ حَفْصِ بْنِ عَاصِمٍ، عَنْ أَبِي هُرَيْرَةَ، قَالَ قَالَ رَسُولُ اللَّهِ صلى الله عليه وسلم ‏"‏ مَا بَيْنَ بَيْتِي وَمِنْبَرِي رَوْضَةٌ مِنْ رِيَاضِ الْجَنَّةِ، وَمِنْبَرِي عَلَى حَوْضِي ‏"‏‏.‏

Sahih al-Bukhari, 7335
Vol. 9, Book 92, Hadith 435
Book of holding fast to the


14/07/2025

Sahl (Mulungu asangalale) adati,

"Mtunda womwe udali pakati pa mimbali (ya Mtumiki ﷺ) ndi khoma la Mzikiti kumbali ya Chibula, unali (mpata) wongokwanira nkhosa kudutsa."

"حَدَّثَنَا ابْنُ أَبِي مَرْيَمَ، حَدَّثَنَا أَبُو غَسَّانَ، حَدَّثَنِي أَبُو حَازِمٍ، عَنْ سَهْلٍ، أَنَّهُ كَانَ بَيْنَ جِدَارِ الْمَسْجِدِ مِمَّا يَلِي الْقِبْلَةَ وَبَيْنَ الْمِنْبَرِ مَمَرُّ الشَّاةِ‏.‏"

Sahih al-Bukhari, 7334
Vol. 9, Book 92, Hadith 434
Book of holding fast to the


13/07/2025

Anas bin Malik (Mulungu asangalale naye) adati,

"Phiri la Uhud lidaonetsedwa kwa Mtumiki ﷺ ndipo Iye adati, "Ili ndi phiri limene limatikonda ndipo limakondedwa nafe. "O Allah! Abraham adaupanga mzinda wa Makkah kukhala (malo) wopatulika, ndipo Ine ndikupanga (Mzinda wa Madina) womwe uli pakati pa maphiri awiri awa kukhala wopatulika.'

حَدَّثَنَا إِسْمَاعِيلُ، حَدَّثَنِي مَالِكٌ، عَنْ عَمْرٍو، مَوْلَى الْمُطَّلِبِ عَنْ أَنَسِ بْنِ مَالِكٍ ـ رضى الله عنه ـ أَنَّ رَسُولَ اللَّهِ صلى الله عليه وسلم طَلَعَ لَهُ أُحُدٌ فَقَالَ ‏"‏ هَذَا جَبَلٌ يُحِبُّنَا وَنُحِبُّهُ، اللَّهُمَّ إِنَّ إِبْرَاهِيمَ حَرَّمَ مَكَّةَ، وَإِنِّي أُحَرِّمُ مَا بَيْنَ لاَبَتَيْهَا ‏"‏‏.‏ تَابَعَهُ سَهْلٌ عَنِ النَّبِيِّ صلى الله عليه وسلم فِي أُحُدٍ‏.‏

Sahih al-Bukhari, 7333
Vol. 9, Book 92, Hadith 433
Book of holding fast to the


13/07/2025

Ibn 'Umar (Mulungu asangalale naye) adati,

"Ayuda anadza kwa Mtumiki ﷺ ndi munthu wa mwamuna ndi wina wamkazi, omwe (awiriwo) adachita chiwerewere (kuti Mtumiki aweruze pakati pawo), ndipo Mtumiki ﷺ adalamula (kuti awiriwo agendedwe miyala mpaka imfa). Ndipo iwo anali kugendedwa pafupi ndi mzikiti pa malo amene Jeneza inali kuikidwa."

"حَدَّثَنَا إِبْرَاهِيمُ بْنُ الْمُنْذِرِ، حَدَّثَنَا أَبُو ضَمْرَةَ، حَدَّثَنَا مُوسَى بْنُ عُقْبَةَ، عَنْ نَافِعٍ، عَنِ ابْنِ عُمَرَ، أَنَّ الْيَهُودَ، جَاءُوا إِلَى النَّبِيِّ صلى الله عليه وسلم بِرَجُلٍ وَامْرَأَةٍ زَنَيَا، فَأَمَرَ بِهِمَا فَرُجِمَا قَرِيبًا مِنْ حَيْثُ تُوضَعُ الْجَنَائِزُ عِنْدَ الْمَسْجِدِ‏.‏"

Sahih al-Bukhari, 7332
Vol. 9, Book 92, Hadith 432
Book of holding fast to the


13/07/2025

Anas bin Malik (Mulungu asangalale naye) adati: Mtumiki ﷺ adapempha kuti,

"O Allah ikani madalitso Anu pa milingo yawo (zinthu zawo), ndipo dalitsani Sa' ndi Mudd yawo"

(Mtumiki ﷺ) amatanthauza anthu aku Madina.

حَدَّثَنَا عَبْدُ اللَّهِ بْنُ مَسْلَمَةَ، عَنْ مَالِكٍ، عَنْ إِسْحَاقَ بْنِ عَبْدِ اللَّهِ بْنِ أَبِي طَلْحَةَ، عَنْ أَنَسِ بْنِ مَالِكٍ، أَنَّ رَسُولَ اللَّهِ صلى الله عليه وسلم قَالَ ‏"‏ اللَّهُمَّ بَارِكْ لَهُمْ فِي مِكْيَالِهِمْ، وَبَارِكْ لَهُمْ فِي صَاعِهِمْ وَمُدِّهِمْ ‏"‏ يَعْنِي أَهْلَ الْمَدِينَةِ‏.‏

Sahih al-Bukhari, 7331
Vol. 9, Book 92, Hadith 431
Book of holding fast to the


Want your school to be the top-listed School/college in Pretoria?

Click here to claim your Sponsored Listing.

Location

Website

Address


Pretoria