09/01/2026
Bwalo la Supreme ku Blantyre lakana kumva pempho la mlembi wamkulu wa chipani cha MCP a Richard Chimwendo Banda, lofuna kuti asiye kusungidwa kundende podikilira mlandu oganiziradwa kufuna kupha munthu.
Oweruza Dorothy Nyakaunda wapereka chigamulochi ponena kuti pempholi lafulumira kufika ku bwalo la Supreme, chifukwa ati bwaloli limamva nkhani zimene zagamulidwa ku bwalo lalikulu.
Chigamulochi chadza mokomera mbali ya boma, imene inapempha bwalo, ati pozindikira kuti pempholi linalo ndi zolakwika.
Zateremu ndiye kuti a Chimwendo Banda akusungidwabe ku ndende podikilira siku la mlandu wawo, ndipo a Khwima Mchizi oimira a Banda, atsimikiza kuti a Chimwendo Banda akudwala.
Mchithunzimu a Khwima Mchizi
Wolemba Daniel Zimba
03/06/2025
27/04/2024
22/04/2022