Tipange dawah by professor hassan said Zambia minikaa

Tipange dawah by professor hassan said Zambia minikaa

Share

KUNGOKUMBUTSANA ZAMBIRI ZACHISLAM

07/06/2022

Salaam alaikum

16/05/2022

Kwa anthu amene mumafusa kuti gulu lino lilipo Ku WhatsApp yankho gulu lino kulibe Ku WhatsApp app

05/05/2022

TIYENI TIMUFUNSE YESU MWINI ATIUZE ZOONA

Kwa nthawi yaitali takhala tikutsutsana pa nkhani ya Yesu.Ndipo tinaganiza kuti ndi bwino kuti timve zoona zenizeni kuchokera kwa Yesu mwini wake.Ndipo iye anapereka mayankho momveka bwino motere:

Ndaona Malemba: Kodi a Yesu ndinu ndani?
Yesu: Ndine munthu(Yohane 8:40)

Ndaona Malemba: Kodi m***a kuchita chilichonse?
Yesu: Ayi,sindingathe kuchita kalikonse mwa ine ndekha(yohane 5:30)

Ndaona Malemba: Kodi ndinu Mulungu?
Yesu: Mwatani kodi,ndakuuzani kuti ndine munthu(Yohane 8:40)ndiye ndikhalanso bwanji Mulungu? Ine ndi mneneri wa Mulungu(Mateyu 13:57)

Ndaona Malemba: Ayi,Yesu koma ambiri amati ndinu Mulungu.
Yesu: Ayi,ine ndine mneneri wa Mulungu(Luka 13:33)

Ndaona Malemba: Nanga iwo amene amati ndinu Mulungu amakunamizirani?
Yesu: Iwo amene amati ndine Mulungu amapembedza mwachabe,ndipo chiphunzitso chawo ndi chochokera kwa anthu osati kwa Mulungu(Mateyu 15:9)

Ndaona Malemba: Nanga bwanji anthu amati ophunzira anu monga Paulo munawauza kuti ndinu Mulungu?
Yesu: ine? komanso anakuuza kuti Paulo ndi ophunzira wanga ndani? Ngati mukufuna kudziwa choonadi funsani ophunzira anga monga Petulo ndi ena aja.

Ine chabwino ndikukafunsa kwa Petulo,sindikufunanso chilichonse kuchokera kwa Paulo.

Ndaona Malemba: Petulo,eti Yesu ndi ndani?
Petulo:Yesu ndi mneneri wa Mulungu,ndipo Mulungu anachita zambiri zamphamvu ndi zodabwitsa kuzera mwa iye(Machitidwe 2:22)

Ndaona Malemba: a Petulo ndili ndi zambiri zoti ndikufunseni.
Petulo:Bwanji tidzakumanenso tsiku lina,chifukwa ndikuthamangira kumtundaku mkulu winawake dzina lake Paulo akuuza anthu zomwe Yesu sanaphunzitse,iye akufuna kusocheretsa anthu(Agalatiya 2:11)

05/05/2022

A salaam alaykum ,asilam tiyeni tizitenga nowo mbali pazonsezi pano osaiwala kupanga like ndi comment kuti tidziwe kuti mukusatila za Dawah zi

05/05/2022

25 DECEMBER NDI TSIKU LIMENE
ANABADWA MITHRA, mulungu wa
dzuwa.

MCHIKHALIDWE CHACHIKUNJA
CHA CHI ROMA, LINASINTHIDWA
KUKHALA TSIKU LOBADWA YESU,
NGAKHALE KUTI BAIBULO LIDALOSERA NDI
KULETSA KUKONGOLETSA MTENGO
WA KHRISMAS MU
YEREMIAH 10:2-5.
IZI ZINACHITIKA PA MSONKHANO WA KU
NICEA MCHAKA CHA 325 AD , ZAKA
ZOPITIRILA MAZANA ATATU YESU
ATACHOKA KALE.

UDAYAMBIKA ND MKULU WINA
WOTCHEDWA ATHANIUS,
DIKONI WA MU IGUPUTO/Egypt WOCHOKERA KU
ALEXANDRIA ; NDI YEMWENSO
ADAKONZA ZA UTATU WA MULUNGU (trinity)
NDIPO UDABVOMEREZEDWA PA
MSONKHANOWU.

SABATA INASINTHIDWA
M'MALO MWAKE ANAIKA
Sunday PA MSONKHANOWU.

CHIFUKWA
CHAKUTI CHIKHRISTU CHIDASIYA ZOMWE
ZIDALI PHATA LA CHIPHUTSITSO CHA
YESU (a.s)
MULUNGU ANATUMIZA
MUHAMMAD 'SAW' KUTI ADZAPHUNZITSENSO
CHIKONZERO CHAKE
CHOYAMBA NDI KUBWEREZA M'MALO
ZONSE ZIMENE ZINASINTHIDWA;
KALENDALA YACHIROMA YOTCHEDWA
JULIAS YOMWE IDAYAMBITSA CHAKA cha CHIKHRISTU, NYAMA YA NKHUMBA
INALOLEDWA: MDULIDWE
UNATHETSEDWA NDI PAULO MU
AGALATIYA 5:2. (taonani ine paulo
ndinena ndi inu kuti ngati mulola
akuduleni , khristu simudzapindula naye
kanthu) ..TAONANI PA 1 PETRO4:16 -
koma ngati mumwa zowawa chifukwa
chakuti ndinu Akhristu, musachite
manyazi, koma mulemekeze Mulungu
chifukwa cha dzinalo...

05/05/2022

BODZA LA M'BAIBULO LIKUONEKERA POYERA

Mateyo 28:18 Yesu adadza pafupi nawauza kuti, MPHUMVU ZONSE ZAPATSIDWA KWA INE KUMWAMBA NDI PANSI PANO.
Marko 13:32 Koma za tsiku lake kapena nthawi yake, palibe amene amadziwa.
▸ NGAKHALE INEYO {YESU} MWANANE SINDIDZIWA ◂ , Amadziwa ndi Atate okha basi.
FUNSO ▾ ▾
FUNSO LIKUPITA KWA AMENE AMAZICHA KUTI AKHRISTU!
Ngatidi zili zoona kuti Yesu adapasidwadi mphamvu ZONSE ndi chifukwa chiyani Mulungu SADAMPETSE Yesu mphamvu zozindikira tsiku la chimaliziro ???
▴ ▴
Akhristu funso ndi limeneli lofunika kuti inuyo muyankha Osati za mutu pano ayi !

05/05/2022

AKHRISTU MUMATI ASILAMU SAMADZIWA KUMASULIRA KWA BAIBULO
CHONDE BWERANI MUZATIMASULILE PAMODZI NDI KUYANKHA
MAFUNSOWA PANO
Ndiyambe ndi Quran 7:162 Koma anthu oipa amene adali pakati pawo,(akhristuwa) ADASITHA MAWU AMENE ADAPATSIDWA....
(Ndichifukwa chake Baibuloli lilichonchi lero lino)
Maso palemba akhristu tiyenitiyeni !
2 Mafumu 24:8 Yehoyakini anali wa ZAKA 18 pamene adalowa ufumu, ndipo adalamulira miyezi ITATU ku Yeresalemu.
2 Mbiri 36:9 Yehoyakini anali wa ZAKA 8 pamene adalowa Ufumu, ndipo adalamulira miyezi ITATU NDI MASIKU KHUMI ku Yerusalemu.
1* FUNSO LOYAMBA; Yehoyakini anali wa ZAKA 8 kapene 18 pamene adalowa ufumu mu Yerusalemu ???
2* FUNSO LACHIWIRI; Yehoyakini adalamulira miyezi ITATU kapena miyezi ITATU ndi MASIKU KHUMI ku Yerusalemu ?????
Mafunso awiriwa achokera mu Baibulo la King James Version

04/05/2022

Salaam alaykum

15/12/2021

Christopher Allan mothandizana ndi Gerald E. Weston* anayambisanso mpingo wawo *Living Waters* kwa *America* komweko nawonso unabwera ndi *malilime* komanso *dance kukopa anthu ndi kuvina). Udayamba pa 24th September 1988 ku North Carolina ku Southeastern region of the United States.

*Koma mipingo yonseyi inatuluka mumpingo umodzi wa Chikatorika.*

*Mipongo yonseyi ndi yogalukila (yowukila) mpingo wa Akatolika.*

*KING HENRY VIII* pamene amafuna kupangisa ukwati wake ku chiroma, anamkana chifukwa mkazi wake woyamba anasiyana chifukwa cha chigololo ndiye pa chikhulupiliro cha akatorika sadalisanso ukwati otero koma ngati mmodzi wa iwo akamwakira tsono bambo *AMSRONG:....*

Poona kuti akatolika akumkana kumudalitsira ukwati wake kenako mkuluyu anayambisanso mpingo wake wa *ANGLICAN CHURCH* umu munali muchaka cha 1534, ku England.

Zochita za Anglican ndi akatolica ndi zofananako koma ma member aku Anglican Church amakwatira pamene ku Catholic sakwatira.

15/12/2021

ASALAAM ALAYKUM
Takulandilani kuno Ku page Yaaaaa professor said hassan Zambia yomwe timakumbutsana zokhudza bible komanso qur aan Muno timatenga mitu for example mutu ngati akhristu ndi asilam ndi ndani amasatira bible ndiye timayambano
Kupeleka mavess
Muno zamutu Muno Ayiiiii

15/12/2021

MUKAFUKUFUKU WATHU IF A GROUP YA MFUNDO ZA TAHWEED ISLAMIC DAWAH GROUP.

TAPEZA KUTI MIPINGO YONSEYI IMENE ILI PA DZIKO LINO LA PANSI NDI YOYAMBITSA ANTHU WAMBA CHABE.

Ndi mipingo imene anayambisa anthu monga mmene amayambisira club ya mpira ngati awa:

*MARTINE LUTHER;* anayambisa mpingo wa *LUTHERANE CHURCH* ku England chaka cha 1896.

*PASTOR LAZAEL STANDISH* anayambisa mpingo wake wa *MBONI ZA YAHOVA* Mu chaka cha 1914.

Bambo *WILLIAM SMITH NDI MAI ELLAN G. WHITE* anayambisanso mpingo wawo wotchedwa *SEVENTH DAY ADVENTIST CHURCH* Mu chaka cha 1863,

Kenako munazabuka mkangano kusagwiriza muzochitika, izi zinachititsa mpaka kugawikana magulu anayi
(4) gulu lina linatchedwa,

*SEVENTH DAY TRUE VISION*

Lina *SEVENTH DAY BAPTIST*

Lina *SEVENTH DAY* Awa amakanilatu azimayi kuyima ku Guwa kulalikira pa maso amuna.

Bambo *LEONARD GAPBEL* anayambisanso mpingo wake wa *DUTCH REFORMED CHURCH* (1571 ku Netherlands)

*DR DAVID LIVINGSTONE* anayambitsa mpingo wake wa CCAP mucha cha 1876.

Iye adali atangobwera kumene kuchokera ku *Scotland* kumene Iye adali kupemphela mu mipingo wa *Free Church of Scotland*

Sizinamuyendele kumenekuja ndipamene adaganiza zobwela kuno ku Africa adakayambirila ku Zambia, kukayambitsa mpingo wake nawutcha *CCAP*
*Church of Central Africa Presbyterian*

Mpingo umenewu nthawi zina umaziwika ndi dzina loti; *The Livingstonia Synod*

*CCAP,* Kutanthauza kuti; *Church of Central Africa Presbyterian* mpingo umenewu ukupezeka pakati pa Africa ku Malawi, Zambia, ndi Zimbabwe basi, mmaiko azungu kulibe.

*DR DANIEL SHEVA* anayambisanso mpingo wake *ASSEMBLES OF GOD* unayambikira kwa *America* ndi mpingo umene umene unayambitsa zachilendo monga *malilime* komanso *dance* (kuvina). Umu munali mucha cha 1914.

*Christopher Allan mothandizana ndi Gerald E. Weston* anayambisanso mpingo wawo *Living Waters* kwa *America* komweko nawonso unabwera ndi *malilime* komanso *dance kukopa anthu ndi kuvina). Udayamba pa 24th September 1988

Want your school to be the top-listed School/college in Zomba?

Click here to claim your Sponsored Listing.

Location

Category

Website

Address

Zomba