Tinada nkhawa kwambiri
Yesu Ali ndi zaka 12, Yosefe ankatengaso banja lake kupita ku Yerusalemu. Inali nthawi ya chikondwelero Cha pasika ndipo mabanja akuluakulu amayendera limodzi. Ankayenda ndi nyama zonyamula katundu ndipo anadutsa mnjira zomwe zinali ndi msipu wobiriwira m'mbali mwake. Aluyandikira mzinda wa Yerusalemu, womwe unali pamalo okwera, n'kutheka kuti ambiri anayamba kuimba masalimo a nyimbo zokwerera ku mzinda. ( Sal 120-134 ) Pa nthawi ya chikondwelerochi, mumzindawu munali piringupiringu. Chikondwelerocho chitatha, mabanja onse anayamba ulendo wobwerera kwawo. Mwina chifukwa chotanganidwa, Yosefe ndi Mariya ankaona Ngati Yesu Ani naye limodzi pa ulendowo ndipo akuyenda ndi achibale ena. Koma atayenda nmtunda wa tsiku lathunthu, anazindikira kuti Yesu wasowa. Luka 2:41-44.
Nthawi yomweyi anayambaso ulendo wobwerera ku Yerusalemu ndipo anafufuza mmalo onse amene anadutsa. Taganizirani mmene mzindawo unkaonekera pa nthawiyi, anthu onse atapita, pamene Iwo ankayenda kwinaku akuitana Yesu. Kodi iye anali Ali kuti? Atafufuza kwa masiku atatu, mwina Yosefe anayamba kuda nkhawa kuti walephera udindo wake umene Yehova anamupatsa. Kenako anapita kukafufuza mkachisi. Iwo anafufuza paliponse mpaka anafika mchipinda chimene munali aphunzitsi odziwa bwino chilamulo ndipo mmenemo ndi mmene anampeza Yesu. Apa zoonekeratu kuti mtima wa Yosefe ndi Mariya umakhala Malo. Luka 2:45,46.
Yesu ankambetsetsa zimene aphunzitsiwo anakanena ndiponso ankawafunsa mafunso. Aphunzitsiwo anachita chidwi kwambiri ndi nzeru za mwanayo komanso mayankho amene ankapereka. Koma Mariya ndi Yosefe anadabwa kumpeza Ali kumeneko. Baibulo limasonyeza kuti Yosefe sanalankhure kanthu. Koma mawu amene Mariya analankhula akasonyeza maganizo amene makolo onsewo anali nawo. Iye anati: " mwanawe, m'chifukwa chiyani wativutitsa chonchi ? Ine ndi bambo Akowa tinada nkhawa kwambiri ndipo timakufunafuna." Luka 2:47,48.
Si ntchito yamasewera, ngakhare mwanayo atakhala wangwiro. Zimene zikuchitika m'dzikoli masiku ano zikuchititsa kuti kulera ana kuzipangitsa makolo kukhala ndi 'nkhawa kwambiri. ' komabe Iwo ayenera kudziwa kuti Baibulo limasonyeza mavuto amene akukumana nawo.
N'zosasangalatsa kuti Yesu anali pamalo amene ankaona kuti amuthandiza kuyandikira kwambiri kwa atate wake wakumwamba, Yehova. Iye anali ofunitsitsa kuphunzira zambiri za atate wake. Mchifukwa chake anayankha Malo ake kuti : " mumandifunafuna chifukwa chiyani? Kodi simunadziwe kuti ndiyenera kupezeka mnyumba ya atate wanga ? Luka 2:49.
Yosefe ayenera kuti anaganizira mawu amenewa kambirmbiri mawuwa ankanyadira popeza anali atayesetsa kumuphunzitsa mwanayu kuti aziona kuti Yehova Mulungu ndi atate wake. Ngakhare kuti Yesu anali adakali mwana, ankakonda kwambiri Yehova ndipo
Ankamuona kuti ndi atate wake. Iye anakhala ndi maganizo amenewa chifukwa Cha zimene Yosefe ankaphunzitsa.
Ngati ndinu bambo, Kodi mumazindikira udindo umene muli nawo wothandizira ana anu kuti aziona kuti Yehova ndi atate wachikondi komanso amateteza anthu ake ? Nchimodzimodziso munalera ana oti si anu. Muyenera kutengera chitsanzo Cha Yosefe ndipo muziona kuti mwana aliyense ndi ofunika athandizeni kuyandikira kwa Atate wawo wakumwamba Yehova Mulungu. Aefeso 6:4.
nkhani kuchokera mau a Mulungu tiphunzire ndikuchitapo kanthu
Contact information, map and directions, contact form, opening hours, services, ratings, photos, videos and announcements from nkhani kuchokera mau a Mulungu tiphunzire ndikuchitapo kanthu, Tutor/Teacher, kabudula primary school p. o box 20, nsalu, Lilongwe.
------created by mcdad-----
ππlead the stories like, comment and share to your friends ππ
chakudya Cha moyo wachikhristu ndiwo mau a Mulungu
---- Afilipi 4:13 ----
- Ndikhoza zonse mwa iye wondipatsa mphamvu
Praise and worship song mixed dance
Hoza weekend
Pa chiyambi panali ndipo mau anali kwa Mulungu ndipo mauwo ndiye Mulungu ( Yohane 1:1 )
anthu timafuna kuyankhulidwa ndi Mulungu mu njira yomwe timaganiza kuti ndiwabwino kwa ifeyo, koma timaiwara kuti kuyankhula kwa Mulungu pa moyo wanu kuli mu Baibulo chifukwa mu Baibulo ndiye momwe muli mau a Mulungu.
06/12/2025
Ine ndiwapemphelera Iwo, sindipemphelera dziko lapansi, koma Iwo amene mwandipatsa ine.
https://www.facebook.com/profile.php?id=61583099199264
Read, comment, like and share the group to your friends
nkhani kuchokera mau a Mulungu tiphunzire ndikuchitapo kanthu
------created by mcdad-----
ππlead the stories like, comment and share to your friends ππ
chakudya Cha moyo wachikhristu ndiwo mau a Mulungu
---- Afilipi 4:13 ----
- Ndikhoza zonse mwa iye wondipatsa mphamvu
Ndikhoza kuchita zonse mwa iye wondipatsa mphamvu. Paja ndi verse yanj imeneyi ?
Yosefe ankasamalira banja lake
Zikukuoneka kuti banjali silinakhalitse ku iguputo chifukwa pasanapite nthawi mngelo anauza Yosefe kuti herode wafa. Choncho Yosefe anatenga banja lake nkuyamba ulendo wobwerera kudziko lakwawo. Ulosi wina unaneneratu kuti Yehova adzaitana mwana wake " kuti atuluke mu iguputo," ( mat. 2:15 )
Yosefe anathandizira nawo kuti ulosi umenewu ukwaniritsidwe. Koma Kodi tsopano iye ndi banja lake akakhala kuti ?
Ngakhare kuti Herode anali atafa, Yosefe anachita zinthu mosamala chifukwa anamva kuti arikelao, amene analowa mmalo mwa Herode, nayeso anali wankhanza . Mulungu anatsogolera Yosefe ndi banja lake kuti apite chakumpoto, kutali ndi mzinda wa yerusalemu , mpaka anafika kwawo ku nazareti Mariya anaberekaso ana ena. ( Mateyu 2:19-23 )
Iwo ankakhala moyo wosalira zambiri komabe ankafunika akugwira ntchito mwakhama kuti apeze zofunika pa moyo. Baibulo limanena kuti Yosefe anali mmisiri wamatabwa. Mawu amenewa kuti ntchito yake inkaphatikizapo kugwetsa mitengo, kuinyamula komaso kuiumitsa kuti akamangire nyumba ndi milatho ing'onoing'ono . Mitengoyi ankagwiritsaso ntchito popanga maboti, ngolo,mateyala,magoli ndi zipangizo zosiyanasiyana zaulimi. ( Mat. 13:55 ) Imeneyi sinali ntchito yamasewera. Nthawi zambiri mmisiri wamatabwa ankagwirira ntchito pakhonde pa nyumba yake kapena m'kanyumba komwe ankamanga moyandikana ndi nyumba yakeyo.
Yosefe anali ndi zipangizo zosiyanasiyana ndipo n'kutheka kuti Zina mwa zimenezi anapatsidwa ndi bambo ake. Ankagwiritsa ntchito zipangizo monga sikweya, chingwe choongolera, kankhwangwa, sowo, kasemasema, hamala, tchizulo, zomatira zosiyanasiyana, chobowolera komanso mwina ankakhala ndi misomali ngakhare kuti inali yokwera mtengo.
Yesu Ali wang'ono ayenera kuti ankakonda kuonerera bambo ake akamagwira ntchito. Ankayang'anitsitsa mwachidwi chilichonse chimene Iwo ankachita. Ayenera kuti ankachita chidwi ndi mphamvu komanso luso la bambo akewo. N'kutheka kuti Yosefe ankaphunzitsa mwana wakeyo ntchito zing'onozing'ono monga kusalaza thabwa pogwiritsa ntchito chikopa chouma Cha nsomba. Mwinaso anamuphunzitsa kusiyanitsa matabwa a mitengo imene ankagwiritsa ntchito, monga matabwa a mitengo wa mkuyu, wa maolivi ndi mitengo ina.
Yesu ankadziwa ngakhare kuti bambo ake anali ndi manja okhakhala chifukwa Cha ntchito imene ankagwira, monga kugwetsa mitengo, kuiwaza komanso kulumikiza matabwa, Iwo ankamusisita mwachikondi ndiposo ankamulimbikitsa. Ankachitaso chimodzmodzi ndi mayi ake komanso abale ake. Yosefe ndi Mariya anali ndi banja lalikuru chifukwa m'kupita kwa nthawi anabereka ana ena osachepera 6, kuwonjezera pa Yesu ( mat. 13:55,56 ) choncho Yosefe ankafunika akugwira ntchito mwakhama kuti azisamalira ndiponso kudyetsa banja lakeli.
Komabe it's ankadziwa kuti chofunika kwambiri ndi kusamalira banja lake mwauzimu. Choncho ankayesetsa kupeza nthawi yophunzitsa ana ake za Yehova Mulungu ndi malamulo ake. Nthawi zonse Yosefe ndi Mariya ankatenga ana awo kupita kudunagoge kumene chilamulo chinkawerengedwa ndiponso kufotokozedwa. N'kutheka kuti Yesu ankakhala ndi mafunso pa zimene wamva kudunagogeko ndipo Yosefe ankayesetsa kumuyankha mafunso akewo. Yosefe ankatengaso banja lake kupita ku zikondwerero zomwe zinachitika ku Yerusalemu. Kuti akapezeke ku mwambo wa pasika umene unkachitika chaka chilichonse, iye ndi banja lake ankayenera kuyenda ulendo wa makilomita 110. Ulendo wonsewu munatenga Mulungu iwiri.
Masiku ano, Akhristu omwe ndi mitu ya mabanja amachitaso chimodzmodzi. Amadzipereka kuthandiza ana awo ndipo amaona kuti kuphunzitsa anawo zinthu zauzimu nkofunika kwambiri kuposa zinthu zathupi. Iwo amyesetsa kupita ndi ana awo ku misonkhano yonse ya mpingo ngakhareso yayikuruikuru. Mofananana ndi Yosefe, Iwo amadziwa kuti Palibe chabwino chimene angapatse ana awo kuposa kuwaphunzitsa zinthu za uzimu.
Click here to claim your Sponsored Listing.
Location
Category
Website
Address
Lilongwe
Opening Hours
| Monday | 09:00 - 17:00 |
| Tuesday | 09:00 - 17:00 |
| Wednesday | 09:00 - 17:00 |
| Thursday | 09:00 - 17:00 |
| Friday | 09:00 - 17:00 |
| Saturday | 09:00 - 17:00 |
| Sunday | 09:00 - 17:00 |