02/06/2026
Kusuta ndi haram chifukwa kumaononga moyo komanso kumaononga zambiri pa moyo wa munthu
"The Quran and Sunnah according to the Understanding of the Pious Predecessors"
02/06/2026
Kusuta ndi haram chifukwa kumaononga moyo komanso kumaononga zambiri pa moyo wa munthu
01/06/2026
Shirk imatanthauza kuphatikiza Allah ndi zithu zina pa zomwe ziri za Allah yekha-ngati kupembedza, kupempha, kapena kukhulupirira kuti wina ali ndi mphamvu ngati za Allah.
Magulu ena ama Sufi amachita zinthu zomwe ndi shirk, monga;
1.Kupempha ndi kupembedza manda a anthu olungama.
- Amapita kumanda a waliy, sheikh, kapena mtumiki, namupempha kuti amupatse mwana, ndalama, machiritso ndi zina zotero.
- Amati “E iwe sheikh, ndithandize, ndipulumutse”. Izi ndi pempho kwa wakufa, ndipo pempho ndi mtundu wa kupembedza. M’Chisilamu kupembedza kumayenera kukhala kwa Allah yekha.
Qur’an: _“Musapembedze wina aliyense pamodzi ndi Allah”_
2. Kupempha thandizo kwa anthu amoyo kapena akufa omwe palibe kuthekera.
- Kukhulupirira kuti ma sheikh ali ndi mphamvu yoyendetsa dziko, kudziwa zobisika, kuthandiza popanda chilolezo cha Allah.
- Izi zimafanana ndi kunena kuti pali wina wodziwa za mtsogolo ndi wotha kupanga zinthu kufanana ndi Allah, zomwe ndi shirk mu Rububiyyah.
3. Kubzola malire pakukonda anthu olungama;
- Kuwapatsa makhalidwe a umulungu, kuwalambira, kuyatsa nyali pamanda awo, kupereka nsembe kwa iwo, kupanga zikondwerero chifukwa cha iwo komanso kuzungulira manda awo.
- Chiyambi cha kupembedza mafano m’mbiri chinali chonchi: anthu anayamba kulemekeza anthu abwino mopitirira muyeso mpaka anayamba kuwapembedza.
4. Bidi'a ndi mapemphero omwe sali mu Sunnah;
- Kupanga mapemphero kwa anthu ena, kunena mayina a ma sheikh m’malo mwa dzina la Allah, kuvina, kuimba ndi kuganiza kuti ndi kupembedza.
- Akatswiri amati ngati chinthu chachitidwa ngati kupembedza koma sichinatsimikizidwe ndi Mtumiki ﷺ, chimakhala bid’ah, ndipo chikapitirira chimatha kutsogolera ku shirk.
Chofunika kudziwa:
Sima sufi onse ali chimodzimodzi. Pali ena omwe amakhala makafiri kamba kopanga kwawo shirk , pomwe ena amakhala asilamu komano opandukira malamulo a Allah ndi mtumiki wake kamba kopanga kwawo zomwe Allah ndi mtumiki wake sanalamule (bidi'ah).
Malawian Arabic Teacher
01/06/2026
Ndipo nkhani imeneyi ofunika kuyimva bwino lomwe, sheikh akufotokoza zokhudzana ndiubwino okwatira monga tonse tikudziwira kuti pali thawi inayake mwamuna amafunikira mkazi komanso mkazi amafunikira mwamuna, ndipo kwamene tili ndikuthekera tiyeni tikwatire thawi ndiyomweyi, tisamangoti ndipeze kaye ndalama yokwanira ndikwatira masiku ndikumapita, m'bale wanga dziwa kuti kusaka mariziq sikungathe, ndipo sikudzatha mpaka tidzamwalira, tiyeni tikwatire.
01/06/2026
Kodi mtendere wa m’moyo wa banja ungakwaniritsidwe bwanji?
Kukhala ndi mtendere m’banja kumafuna khama ndi mgwirizano wa onse awiri omwe kwatirana. Nawo malangizo omwe angathandize kukwaniritsa mtendere m’banja:
1. Kulankhulana bwino: Okwatirana ayenera kulankhula m***a mtima komanso momvetsetsa bwino za maganizo ndi zosowa zawo. Kumvetsera mwatcheru ndi kumvetsetsana kungachepetse kusamvana ndi mikangano.
2. Kulemekezana: Okwatirana ayenera kulemekezana, ngakhale pa nthawi ya mkangano. Ulemu umamanga chikhulupiriro ndi kulimbitsa ubwenzi pakati pawo.
3. Kugwirizana ndi kumvetsetsana: Ukwati ndi mgwirizano. Aliyense ayenera kuyesetsa kugwira ntchito ndi mnzake kuti akwaniritse zolinga zomwezo. Kugwirizana polimbana ndi zovuta kumalimbitsa ubale.
4. Kukhululirana ndi kunyalanyaza zolakwa: Palibe okwatirana opanda zolakwa. Kukhululirana ndi kunyalanyaza zolakwa kungathandize kudutsa mavuto ndi kulimbitsa mtendere.
5. Kusamala zinthu zing’onozing’ono: Zinthu zing’onozing’ono, monga mawu okoma ndi mphatso zodabwitsa, zingalimbikitse kumva kuti ukuyamikiridwa ndi kukondedwa pakati pa okwatirana.
6. Kupatsa mnzako nthawi: Okwatirana ayenera kupatula nthawi yochita zinthu pamodzi ndi kusangalala wina ndi mnzake, zomwe zimalimbitsa ubale wamalingaliro.
7. Kugwirizana polera ana: Ngati muli ndi ana, okwatirana ayenera kugwirira ntchito limodzi powalera, zomwe zimalimbitsa kumva kuti muli umodzi komanso mgwirizano.
8. Kuyamikirana: Okwatirana ayenera kufotokozera wina ndi mnzake kuyamika kwawo, zomwe zimalimbitsa kumva kuti ukuyamikiridwa ndi kukhala ndi mtendere.
Pogwiritsa ntchito malangizowa, okwatirana angalimbikitse mtendere m’banja lawo ndi kumanga ubale wa ukwati wamphamvu komanso wokhalitsa.
Allah awadalitse onse omwe ali pa banja la halal 🤲.
31/05/2026
Shirk idayamba mwa anthu a Nowa chifukwa cha kubzola malire pa anthu olungama.
👉 Njira ya Satana Ibilisi ndi imodzi mwa njira zakale ndi yatsopano, amabwera kwa anthu kuchokera pa chitseko cha kubzola malire pa anthu olungama, kuti muziwatamanda mopitilira muyezo.
Allah adati:
{ إِنَّ الَّذِينَ تَدْعُونَ مِنْ دُونِ اللَّهِ عِبَادٌ أَمْثَالُكُمْ فَادْعُوهُمْ فَلْيَسْتَجِيبُوا لَكُمْ إِنْ كُنْتُمْ صَادِقِين }
{Ndithudi amene mukuwapembeza osakhala Allah ndi akapolo ngati inu, choncho aitaneni,ndipo akuyankheni ngati inu mulidi oona (pazimene mukunenazi)
{ وَالَّذِينَ تَدْعُونَ مِنْ دُونِهِ لَا يَسْتَطِيعُونَ نَصْرَكُمْ وَلَا أَنْفُسَهُمْ يَنْصُرُون }
{Ndipo amene mukuwapembedza osakhala Iye ( Allah ), sangathe kukupulumutsani, ngakhale iwowo sangathe kudzipulumutsa okha}
Mavesi otere amene amathyola ndikuwononga shirk ndi kuwayankha eni ake omwe amapangawo, ndi ochuluka m’Qur’an kwa amene amaganizira ndi kumvetsa. Koma anthu awa samaganizira Qur’an. Zili ngati Qur’an ikulankhula ndi ena osati iwo. Amawerenga ndi kusunga pamtima, koma samaganizira. Motero ndichifukwa chake amapanga shirk ( kumphatikiza Allah ndi zithu zina ).
Ndipo Qur’an imaletsa shirk, ndikuzifunsa zomwe akuzitamandirizo, koma iwo sazizindikira.
[شرح قاعدة جليلة في التوسل والوسيلة - ١/٣٦٣]
🖋️ Imam Ash-Shawkani adati:
Munthu aliyense wanzeru amadziwa kuti kukongoletsa kwambiri manda, kuwapachikira nsalu zokongola, kuwayatsira nyali, ndi kuchita khama pakuwapanga kukhala okongola, zili ndi zotsatira pa chikhalidwe cha anthu wamba. Zimenezi zimabala ulemu owapambanitsa ( mandawo ) ndi zikhulupiriro zabodza.
Momwemonso ngati mitima yawo ikakulitsa chinthu china chokhudza amoyo, ndi chifukwa ichi magulu ambiri adakhulupirira umulungu mwa anthu ambiri kutathauza kuti amazipembeza zithu zochuluka zopanda pake.
[الفتح الرباني من فتاوى الإمام الشوكاني - ٣٢٦/١]
Choncho tikuchenjeza ansilam kukhala kutali ndi anthu a shirk pakuti mwaiwo mulibe chabwino kupatula mkwiyo wa AllaMalawian Arabic Teacherer
31/05/2026
30/05/2026
Mwamuna kapena mkazi wa deen amene sanakwatire akufunika azipepha nthawi zonse kuti Allah amupatse bwezi labwino nthawi zonse komanso akhale omuopa Allah ndiwa Aqeedah wabwino.
30/05/2026
Masufi asintha chipembedzo cha Chisilamu ndipo afalitsa shirk ndi kufr m’dzina la kukonda anthu olungama ku Malawi kuno alipo ambiri, South Africa , Tanzania, Sudan komanso m’maiko ambiri a Asilamu. Chifukwa chake ndikofunika kulimbana ndi zigawengazi ndikuwulula mabodza awo.
Masufi anthu Qadria ndi oyipa ndi otayika.
Chenjera, usakhale mmodzi mwamasufi.
29/05/2026
Ngati mmene zilili kuti mkazi sakuyenera kuvala chovala chothina kapena chachifupi kungopatula kwamamuna wake .
29/05/2026
Tiyeni tisangalale mmasiku amenewa, chifukwa ndimasiku athu achisangalale, tidye timwelere komanso timukumbukire Allah, popanga ma ibadah osiyana siyana.