Jesus is Love ❤️❤️
Kukumana ndi yesu m'masiku osiliza.
kuitanila anthu onse ku chipulumutso m'masiku osiliza
Kugona ndichizolowezi, koma kudzuka ndi moyo ndichisomo chachikulu.. Ambuye alemekezeke
01/09/2025
😭😭💔💔Okuba kupita kukaba ndikuwapeza mayi wa mnyumba mwawo basitu kumaliza kuwabela mkuzawaphanso... Rest well mayi mtambo
Good morning, happy Sunday
Happy Sabbath saints....
Verse of the day...
Pelekan verse yanu yokondedwa..
Chivumbulutso 22 vs21.. chisomo cha ambuye yesu chikhale pa oyela mtima onse amen.
30/08/2025
Mwachison ndimowawa tikukengeza za imfa ya a Raphael kamoto omwe ndi amalume awo a mmodzi mwa admin wathu... Rest well sir 🕊️🕊️💔
Moti kumayamika, enanu mulungu kukusiyan kwa 30 minutes ndithu muyaluka, mukukhalila moyo wa zisomo...
Ambuye akukondelenibe🙏🙏
Ambuye!! Enafe tilibe kodalila ndipo timadalila inuyo, chonde musatisiye tingagwe!!
Ambuye mutikondelebe🙏🙏
26/08/2025
😭😭😭💔💔
Apolisi ku Lilongwe amanga mkulu wa mpingo wa Zion mu mzinda wa Lilongwe, a Yohane Mphatso a zaka 19, powaganizira kuti anakwapula mpaka kupha mayi wa zaka 62 yemwe ati amamuchotsa ziwanda.
Mneneri wa polisi ku Lilongwe a Hastings Chigalu wati, mayiyo Alena Banda anapita ku mpingowu omwe uli ku Zankutu mu mzinda wa Lilongwe, kuti akachite nawo mapemphero a madzulo.
Malinga ndi a Chigalu, mapempherowo anali 8 koloko usiku ndipo akulu ampingo ankachititsa mapemphero ochotsa ziwanda, omwe mwa zina amakwapula anthu ofuna kuchotsedwa ziwandawo kuti ziwanda zichoke.
"Mayi Alena omwe anali mgulu lofuna kuchotsedwa ziwanda, ati anakwapulidwa kwambiri kunsana ndipo izi zinapangitsa kuti akomoke. Anthu atathamangira nawo kuchipatala cha Kamuzu Central madotolo anawauza kuti mayi Alena amwalira. Madotolo anakaniza achibale kutenga thupi la mayiyo ndipo anaitumiza nkhaniyi kupolisi," atero a Chigalu.
A Chigalu ati pakadali pano apolisi apeza mitengo iwiri yomwe akulu ampingo ankagwiritsa ntchito kukwapula anthu mu njira yowachotsa ziwanda.
26/08/2025
Khalidwe komati mukakhala pa ubwenzi ndikumatumizilana ma video kapena zithunzi zanu mutavula chonde chepesani!!!
Izi zimapangisa ena kuzipha komanso ena amalowa nazo mmavuto.. ndikhulupilila nkhani ya msikana uyu tonse tikuiziwa ndipo mnyamata yemwe amagawa pamasamba amchezo zithunzi za msikanayu adagwidwa ndikulandila chilango..
Atsikana zisamalileni, mwamuna okukondan sangakuuzeni mutumize maliseche anu...
Click here to claim your Sponsored Listing.
Location
Category
Telephone
Website
Address
Blantyre