Mulungu akuti, "auze anthu anga, Adani sakondweranso pa iwo!"
Apostle Davie itt Luckson
RIVERS OF LIFE INTERNATIONAL 🌍⛪📖
"The seed of salvation"
Aliyense amene akugwiritsa ntchito zolakwa zathu zakale, machimo akale, kapena zolephera zakale ngati njira kuti awononge tsogolo lathu, sapindula mu Dzina la Yesu
Matenda onse owoneka ngakhale achinsisi omwe akhala m'thupi mwanu nthawi yayitali, lero ndikulengeza machiritso mu dzina la Yesu
Mumangozionesa ngati zinthu ziribwino kwa anthu 😭
Koma mkati mwanu mukuvutika pazachuma ..Ambuye akukumbukireni lero mu dzina la Yesu
Ambuye akukumbukireni mwezi uno usanathe ndikukupatsani chozizwitsa chomwe simudzaiwala.
Aliyense amene akugwiritsa ntchito mu ufiti ndalama zanu ndi moyo wanu, ndikulengeza kuti matsenga amenewo asweke m'dzina la Yesu.
ziwapweteka akakuonani mukusangalala, pakuti amayembekezera azikuonani mukungovutika anaiwala kuti Mulungu sathandizira maudani a dziko lapansi
Mulungu emweyo amene wakusungani ndi moyo
Salola kuti moyo wanu ukhale muchamanyazi.
Mulungu anapangitsa Hana kuimba, anapangitsa Sarah kuseka, anachititsa Naomi kusangalala, akupangitseninso inu KUKONDWERA mwezi uno usanathe
Muli pafupi kulira ngati mwana chifukwa Mulungu wayankha Pemphero lanu!
Mawu olakwika omwe Tinawanenera pa Ana athu chifukwa chamkwiyo, Asapindule pano ngakhale M'tsogolo, mu dzina la Yesu
Click here to claim your Sponsored Listing.
Location
Category
Contact the school
Telephone
Website
Address
Blantyre